Anthu ambiri samamvetsetsa za malo a mtengo wa dzindikila chabwino ndi choipa m`moyo mwathu. Nthawi zambiri timaganiza kuti unali mtengo qmwe unalipo kalekale munthawi ya Adamu ndi Eva. Timakhulupirira kuti mtengo umeneyo unali ndi zipatso za poizoni zoti ukangodya yemwe wadyayo amafa. Mwa tsoka, Adamu ndi Eva anadya za mtengowu ndipo anafa. Tikawerenga za nkhaniyi, timaganiza kwa ife, "zinali zomvetsa chisoni Adam ndi Eva kudya chipatso chakuphachi koma tithokoze sitidzaikidwa m`mayeselo ndi mtengo ngati umenewo". Zachisoni, tikhala tikulimbana ndi mtengo umenewu ndi zipatso zake. Chomwe tiyenera kudziwa ndi chakuti za mtengo wa kudzindikira chabwino ndi choipa udakalipobe mpaka lero. Umagwira ntchito m`mayesero kwa ife chimodzimodzi m`mene unapangira nthawi ya Adamu ndi Eva. Umayimilira ngati njira ina ya kwa Mulungu
Dieser Download kann aus rechtlichen Gründen nur mit Rechnungsadresse in A, B, CY, CZ, D, DK, EW, E, FIN, F, GR, H, IRL, I, LT, L, LR, M, NL, PL, P, R, S, SLO, SK ausgeliefert werden.